pawem logo

Bungwe lomenyerera maufulu a wanthu odwala dziko muno la Patient and Community Welfare Foundation of Malawi (PAWEM) lati ndi lokhumudwa ndi mene boma likuzuzira anthu odwala pa chipatala chamchikulu cha boma la Thyolo. Mkulu wa bungwe la PAWEM Kondwani Kucherekana ndiye walankhula izi m'chikalata chomwe bungweli latulutsa pokhudzidwa ndi momwe ntchito yopereka thandizo kwa anthu odwala pa chipatala cha Thyolo zikuyendera. Malingana ndi m'chikalatachi, chipatala cha Thyolo chili ndi ngongole ya magetsi zokwana 200 million kwacha zomwe ati zikhoza kukhudza umoyo wa anthu odwala ngati magetsi atawadulire. Malingana ndi Kucherekana, chipatala cha Thyolo chimathandiza odwala 800,000 koma ati chili ndi mabedi ogona okwana 300 okha zomwe anati ndi mvuto lina lalimkulu pa m'chipatalapo. Pamenepa bungwe la PAWEM lapempha boma kuti liwonjezere ndalama zomwe limapereka pa chipatalacho zogwirira ntchito pa mwezi kuchoka pa 10 million ponena kuti zinthu zinakwera mitengo.